Kukwaniritsidwa Zofuna Za Umoyo Uno Ndi Umoyo Otsiriza

Olemekezeka Habbaan bin Munqiz (Rahimahullah) akusimba kuti Sahaba wina adamufunsa Mtumiki (sallallahu alayhi wasallam) nati "O inu Mtumiki Wa Allah Kodi ndingapereke gawo limodzi m’magawo atatu (one third) a nthawi yanga imene ndiri nayo pokuwerengerani Durood? Mtumiki (sallallahu alayhi wasallam) adayankha nati, Inde ngati ungafune kutero, Ndiponso adafunsa nati kodi ndingaononge magawo awiri m’magawo atatu a nthawi yanga pokuwerengerani Durood? Rasulullah (sallallahu alayhi wasallam) adati inde ngati ungafune.Swahabayo adafunsanso nati kodi ndingaonongere nthawi yanga yonse pokuwerengerani durood? Mtumiki (sallallahu alayhi wasallam) adayankha nati" Ngati ungachite zimenezi, Allah Ta’ala adzakukwaniritsira chirichonse chomwe ukuchifuna kaya za duniya (dziko lapansi) kapena zaku Aakhirat.

Read More »

Njira Ya Sunnah Yopangira Wudhu Gawo lachisanu

12. Tengani madzi m’manja mwanu ndikutsuka dzanja lanu lamanja mpaka mwakasukusuku katatu. Kenako, tengani madzi m’manja mwanu ndikutsuka dzanja lanu lamanzere mpakana mwakasukusuku katatu. Ndi sunnah pamene mukuyamba kutsuka dzanja lanu kuyambira ku zala kumakwezeka mpaka mwakasukusuku, ngati wina wayambira akasukusuku kumatsika m’musi mpaka ku zala kutsuka kudzalandiridwa, komano zikusemphana ndi njira yasunnah yotsukira dzanja.

Read More »

Kuikonzekera Ramadhan

15. Pamene muli m’mwezi wa Ramadhan yesetsani kupanga ntchito zabwino. Hadith ina ikuti, ntchito ina iliyonse yabwino yomwe ungachite mwakufuna kwako (nafil ibaadah) m’mwezi wa Ramadhan (umalipidwa ndi Allah) ngati wachita chinthu cha faradh (chokakamizidwa kuchita) ndipo ngati wachita ntchito ya farad (yokakamizika kuchita) mumwezi wa Ramadan imaonjezeredwa malipiro ake …

Read More »

Njira Ya Sunnah Yopangira Wudhu Gawo lachinayi

9. Welengani duwa iyi nthawi ina iliyonse pamene mukupanga wudhu kapena mukamaliza wudhu. [1] اَللّٰهُمَّ اغْفِرْ لِيْ ذَنْبِيْ وَوَسِّعْ لِيْ فِيْ دَارِيْ وَبَارِكْ لِيْ فِيْ رِزْقِيْ Oh Allah, ndikhululukireni machimo anga, ndipatseni kutakasuka m’nyumba mwanga ndikundipatsa madalitso muchakudya changa. عن أبي موسى الأشعري رضي الله عنه قال أتيت رسول الله صلى …

Read More »

Kuthetsa Umphawi

Sayyiduna Samurah Suwaai (radhwiyallahu anhu), bambo a Jaabir radhwiyallahu anhu akufotokoza kuti, tsiku lina tidali pamodzi ndi Mtumiki (sallallahu alaih wasallam) ndipo kudabwera munthu wina namufunsa Mtumiki (sallallahu alaihi wasallam) kuti, oh Mtumiki wa Allah (sallallahu alaihi wasallam), ndi ntchito (ibadah) iti yomwe ndi yokondedwa kwambiri pamaso pa Allah? 

Read More »

Kuikonzekera Ramadhan

8. Pamene Ramadhan ikubwera komanso tili mkati kati mwa Ramadhan yesetsani kumanena dua yotsatirayi: اَللّٰهُمَّ سَلِّمْنِيْ لِرَمَضَانَ وَسَلِّمْ رَمَضَانَ لِيْ وَسَلِّمْهُ لِيْ مُتَقَبَّلًا O Allaah nditetezeni ine pondifikitsa m’mwezi wa Ramadhan (ndili wa thanzi komanso nyonga ndicholinga choti ndipindule kwambiri m’mweziwu) komanso usamaleni mwezi wa Ramadhan kwa ine (poupangitsa kuti …

Read More »

Njira Ya Sunnah Yopangira Wudhu Gawo lachitatu

6. Chukuchani mkamwa ndikuthira madzi mphuno nthawi imodzi katatu. Kachukuchidwe kamkamwa ndikuthira madzi mphuno kali motere, choyamba tengani madzi mdzanja lanu lamanja, kenako, pogwiritsa ntchito madzi ena, tsukani mkamwa kamodzi otsalawo gwiritsani ntchito kutsuka mphuno, mudzabwereza zimenezi kawiri kotsalako pogwiritsa ntchito madzi ena ulendo wina uliwonse.

Read More »

Kuyankhidwa Kwa Ma Duwa

Umar (radhwiyallahu anhu) akulongosora kuti: Duwa imakhala idakali pakati pa mitambo ndi nthaka (munlengalenga). Siimapititsidwa mpakana kumwamba ngati muduwamo simunawerengedwe Durood (kutanthauza kuti sipamakhala chitsimikizo cha kuyankhidwa kwa duwayo).

Read More »